Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Kodi Nkhani Zimene Zili M’Baibulo Ndi Nzeru za Anthu?

Kodi Nkhani Zimene Zili M’Baibulo Ndi Nzeru za Anthu?

Yankho la m’Baibulo

 M’Baibulo, lomwenso limadziwika kuti Malemba Opatulika, muli mawu ambiri a nzeru. Komabe, taonani mfundo yochititsa chidwi iyi imene ili m’Baibulo: “Malemba onse anauziridwa ndi Mulungu.” (2 Timoteyo 3:16) Pali maumboni ambiri otsimikiza kuti mawuwa ndi oona. Mwachitsanzo, taonani mfundo zotsatirazi:

  •   Palibe munthu amene anaperekapo umboni woona wosonyeza kuti mbiri inayake yotchulidwa m’Baibulo ndi yolakwika.

  •   Anthu amene anauziridwa kulemba Baibulo anali oona mtima ndipo analemba zinthu mosabisa. Zinthu zonse zimene analemba zimasonyezeratu kuti n’zoona.

  •   Nkhani zonse za m’Baibulo zili ndi mfundo imodzi. Mfundo yake ndi yakuti: Mulungu yekha ndiye woyenerera kulamulira anthu komanso kuti kudzera mu Ufumu wake wakumwamba, adzachita chifuniro chake.

  •   Ngakhale kuti Baibulo linalembedwa zaka masauzande ambiri zapitazo, nkhani zimene linanena zokhudza sayansi ndi zolondolabe mpaka pano mosiyana ndi nkhani zina zimene anthu ambiri ankakhulupirira pa nthawiyo.

  •   Zimene anthu olemba mbiri yakale analemba zikusonyeza kuti maulosi a m’Baibulo akukwaniritsidwa.